Mawu a M'munsi
a Mkhalidwe wachisembwere sumalekereredwa pakati pa Mboni za Yehova, monga mmene sunali kuloledwa pakati pa Akristu a m’zaka za zana loyamba. (1 Akorinto 5:11-13) Mosasamala kanthu za izo, olakwawo angapeze thandizo lachikondi kwa akulu a mpingo. (Yakobo 5:14, 15) Mwakulapa mkhalidwe wawo woipa, oterowo angasangalale ndi chikhululukiro cha Mulungu ndi mpingo Wachikristu.