Mawu a M'munsi
a Mu United States, bungwe la Motion Picture Association of America silimalola azaka zapansi pa 17 (kusiyapo ngati atsagana ndi kholo kapena wolera) kuloŵa filimu iriyonse yodziŵika kukhala yosonyeza chisembwere, kapena kuti yoletsedwa. Kaŵirikaŵiri mafilimu otero amawonetsa zinthu zachiwawa, kutukwana, kapena zithunzi zowonetsa kugonana ndi umaliseche. Komabe, kaŵirikaŵiri koposa, kuletsako sikumachirikizidwa, ndipo achichepere amaloledwa kuloŵa.