a Buku lakuti Theological Wordbook of the Old Testament limati: “Mosangalatsa Yobu 26:7 amapereka chithunzi cha dziko lodziŵika panthaŵiyo kuti linali lolenjekeka m’malo opanda kanthu, mwakutero kuyembekezera zodzatulukiridwa ndi sayansi yamtsogolo.”