Mawu a M'munsi
a Kwenikweni, kufufuza kwaposachedwapa kwasonyeza kuti ngakhale achichepere okulirako a m’zaka za kuchiyambiyambi kwa 20 amavutika kwakukulu pamene makolo awo asudzulana. Kusintha kwachiwonekere kwa mikhalidwe ya makolo awo kumaŵadabwitsa, ikusimba motero The New York Times Magazine. Ambiri amaloŵerera m’moyo wazosangulutsa thupi ndi chisembwere, pamene ena amathetsa kupalana ubwenzi kulikonse, ena akumalumbira kuti sadzakwatira konse.