Mawu a M'munsi
a Kukambitsirana kwathu kwazikidwa pa chimene Baibulo limachitcha por·neiʹa, kapena chisembwere choipitsitsa chakugonana. (1 Akorinto 6:9; yerekezerani ndi Levitiko 18:6-22.) Ichi chimaphatikizapo mitundu yonse ya mayanjano achisembwere. Machitidwe ena oipa, monga zisonyezero zoipa, kuwonerera ogonana, ndi kuwona zinthu zamaliseche, pamene kuli kwakuti siziri por·neiʹa, zikhozanso kuvulaza malingaliro a mwana.