Mawu a M'munsi
b Amene anataya unamwali wawo chifukwa cha kugwiriridwa chigololo kapena kugonedwa paubwana angakhale ndi chitonthozo kudziŵa kuti Mulungu amawawonabe kukhala ‘osalakwa ndi owona.’ (Afilipi 2:15) Aliyense amene anachita dama asanapeze chidziŵitso cha malamulo amakhalidwe abwino a Baibulo mofananamo angapeze chitonthozo kudziŵa kuti chifukwa chosonyeza chikhulupiriro m’dipo la Yesu, ‘anasambitsidwa’ pamaso pa Mulungu. (1 Akorinto 6:11) Mkristu amene wagwera m’chisembwere komano walapa mowona mtima ndipo wachira angakhalenso ndi kaimidwe koyera pamaso pa Mulungu. Kaŵirikaŵiri, anzawo amuukwati achikondi, odera nkhaŵa akhala ofunitsitsa kukhululuka m’mikhalidwe imeneyi.