Mawu a M'munsi
a Wolemba mbiri wa m’zaka za zana loyamba Wachiyuda Joseph ben Matthias (Flavius Josephus) amasimba kuti podzafika nyengo imeneyi, akulu a ansembe a Aisrayeli anali kusankhidwa ndi kuchotsedwa ndi nthumwi za Roma kaŵirikaŵiri kamodzi pachaka. Mumkhalidwe umenewu, malo a mkulu wa ansembe anayamba kukhala ntchito wamba yolipidwa ndalama imene inakopa anthu oipa m’chitaganyacho. The Babylonian Talmud imasanja makhalidwe oipa a ena a akulu a ansembe ameneŵa. (Pesaḥim 57a) Nayonso Talmud imasimba za chikhoterero cha Afarisi pakukonda kwawo chinyengo. (Soṭah 22b)