Mawu a M'munsi
a Zowona, mtumwi Paulo analangizadi Akristu ‘kuiŵala zam’mbuyo.’ Koma Paulo panopo anali kunena za ulemerero wake wakale ndi chipambano cha kudziko, zimene tsopano zinali “zapadzala” kwa iye. Sanali kunena za masautso ake akale, amene anasimba mwaufulu.—Afilipi 3:4-6, 8, 13; yerekezerani ndi 2 Akorinto 11:23-27.