Mawu a M'munsi
a Kwamveka kuti thukuta la magazi limachitika nthaŵi zina pamene munthu wapsinjika maganizo kwambiri. Mwachitsanzo, kupsinjika maganizo kotchedwa hematidrosis, thupi limatulutsa thukuta losakanizika ndi magazi kapena mbali zina za magazi kapena madzi ena a m’thupi ophatikizana ndi magazi. Komabe sitingathe kunena mwachindunji zimene zinachitikira Yesu.