Mawu a M'munsi
a Anthu anayesapo kuchirikiza malamulo oletsa zinthu ameneŵa mwa kupotoza Malemba. Ngakhale kuti Baibulo silimanena zinthu ngati zimenezo, wazaumulungu wina wotchuka wotchedwa Tertullian ankaphunzitsa kuti popeza mkazi ndiye anachititsa “tchimo loyamba, ndi manyazi . . . a kutembereredwa kwa anthu,” akazi ayenera “kuyendayenda monga Hava, akumalira ndi kulapa.” Mpaka analimbikira kunena kuti mkazi wokongola mwachibadwa ayenera kumabisa kukongola kwakeko.—Yerekezerani ndi Aroma 5:12-14; 1 Timoteo 2:13, 14.