Mawu a M'munsi
a Ngakhale kuti mawu akuti “moyo umene munthu amayembekezereka kukhala” ndi akuti “utali umene anthu ambiri amatha kukhala ndi moyo” nthaŵi zambiri amatchulidwa ngati amodzi, mawu aŵiri ameneŵa ndi osiyana. Mawu akuti “moyo umene munthu amayembekezereka kukhala” amatanthauza kuchuluka kwa zaka zimene munthu angayembekezere kukhala ndi moyo, pamene mawu akuti “utali umene anthu ambiri amatha kukhala ndi moyo” amatanthauza kuchuluka kwa zaka zimene anthu ena ake paokhapaokha amakhaladi ndi moyo. Motero, chiŵerengero chongoyerekezera cha moyo umene munthu amayembekezereka kukhala chimapezedwa poona utali umene anthu ambiri amatha kukhala ndi moyo.