Mawu a M'munsi
d Chilamulo cha Mose chinalamula kuti mwamuna amene wachimwitsa namwali am’kwatire. (Deuteronomo 22:28, 29) Ngakhale zinali choncho, sikuti zikatero ukwati umangochitika ayi, chifukwa bambo wa mtsikanayo amatha kukaniza. (Eksodo 22:16, 17) Ngakhale kuti Akristu lerolino sali pansi pa Chilamulo, zimenezi zikutitsimikizira za kuopsa kwa tchimo la kugonana ukwati usanachitike.—Onani “Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga” mu Nsanja ya Olonda ya November 15, 1989.