Mawu a M'munsi
a Langizo la Yesu lopereka “kwa Kaisara zake za Kaisara” silinangonena za msonkho wokha ayi. (Mateyu 22:21) Buku lakuti Critical and Exegetical Hand-Book to the Gospel of Matthew, lomwe analemba ndi Heinrich Meyer, limafotokoza kuti: “Mawu akuti [zake za Kaisara] . . . sakutanthauza misonkho ya boma yokha ayi, koma chilichonse chimene Kaisara anayenera kupatsidwa chifukwa chakuti anali wolamulira.”