Mawu a M'munsi
c Si kuti anthu onse amene amachita kuwapezera mwamuna kapena mkazi amakhala osasangalala. Mwachitsanzo, mu nthaŵi za m’Baibulo, Isake ndi Rebeka anachita kuwakonzera kuti akwatirane, ndipo Isake “anam’konda” Rebeka. (Genesis 24:67) Tingaphunzirepo chiyani pamenepa? Tingaphunzirepo kuti sibwino kunyoza miyambo ya kwanuko ngati sikusemphana ndi malamulo a Mulungu.—Machitidwe 5:29.