Mawu a M'munsi
a Anthu oweta agalu akhoza kusankha galu wamwamuna ndi wamkazi oti abereke ana n’cholinga choti anawo adzakhale ndi miyendo ifupiifupi kapena tsitsi lalitali kusiyana ndi makolo awo. Komabe, kusintha kumene kumabwera chifukwa chobereketsa agalu nthawi zambiri kumachitika chifukwa chakuti maselo ena a agaluwo sanagwire ntchito yake. Mwachitsanzo, pali agalu enaake amene amakhala aang’ono kwambiri chifukwa choti minofu yawo yokhala pakati pa mafupa sikula bwinobwino, ndipo mapeto ake agaluwa amakhala ngati abathwa.