Mawu a M'munsi
b Ngakhale kuti mawu akuti “mtundu” agwiritsidwa ntchito kwambiri mu nkhani ino, tiyenera kutchulapo kuti mawu amenewa si ofanana tanthauzo lake ndi mawu akuti “mtundu” amene ali m’buku la m’Baibulo la Genesis. M’Baibulo mawu akuti “mtundu” amatanthauza zinthu za m’gulu limodzi zomwe zikhoza kukhala zosiyanasiyana. Nthawi zambiri, zimene asayansi amati ndi kusintha kwa mtundu wa chamoyo n’kupanga chamoyo china, kwenikweni kumangokhala kusiyanasiyana kwa zamoyo za mtundu umodzi, monga momwe mawuwa akugwiritsidwira ntchito mu nkhani ya mu Genesis.