Mawu a M'munsi
f Kafukufuku wasonyeza kuti kusintha kumene kumachitika m’zamoyo za mtundu umodzi kumakhala kofananafanana ndipo zimati zikasinthasintha n’kufika nambala inayake, sizisinthanso ndipo nambala ya zamoyo zimene zikusintha imayamba kuchepa. Kuchokera ku zochitika zimenezi, Lönnig anakhazikitsa lamulo latsopano la sayansi lonena kuti “zamoyo zimene zimabadwa zitasintha zimakhala zofanana ndi zina zimene zinabadwa zitasinthapo kale.” Kuwonjezera apo, zomera zosinthika maselo zosakwana wani peresenti n’zimene anazisankha kuti achite nazo kafukufuku wowonjezera, ndipo pa gulu limeneli zomera zosakwana wani peresenti n’zomwe anazipeza kuti angazigwiritsedi ntchito pa ulimi weniweni. Zotsatirapo za kusintha maselo a zinyama zinali zoipa kwambiri kusiyananso ndi zomera, ndipo njirayi kenaka anangosiyiratu.