Mawu a M'munsi
a Akatswiri ankhaniyi amanena kuti ngakhale kuti ana ambiri amene anachitidwapo chipongwe choterechi saulula, amachita zinthu zoonetsa kuti zinazake sizili bwino. Mwachitsanzo, mukaona mwana atayambanso mosadziwika bwino kuchita zizolowezi zimene anasiya kale, monga kukodza pamphasa, kusafuna kusiyana nanu, kapena kuopa kukhala yekha, dziwani kuti kalipokalipo. Koma sikuti mukangoona zimenezi basi ndiye kuti mwana wanu anachitidwa zachipongwe. Mufunseni mwana wanu modekha kuti akufotokozereni zimene zikumuvutitsa maganizo kuti muthe kumulimbikitsa, ndi kum’teteza bwinobwino.