Mawu a M'munsi
a Priestley asanatulukire mpweya wa okosijeni, katswiri wina wofufuza mmene zinthu zimapangidwira wa ku Sweden, dzina lake Carl Scheele anatulukirapo mpweyawu koma sanalembe zimene anatulukirazi. Patapita nthawi kuchokera pamene Priestley anatulukira mpweyawu, katswiri winanso wofufuza mmene zinthu zimapangidwira wa ku France, dzina lake Antoine-Laurent Lavoisier, anatchula mpweyawu kuti okosijeni.