Mawu a M'munsi
a Pali zinthu zinanso zimene zimathandiza nyerereyi kukhala m’malo otentha kwambiri. Ili ndi mapulotini apadera m’thupi mwake amene sasungunuka akatenthedwa kwambiri. Ilinso ndi miyendo yaitali yomwe imaithandiza kuti isamayandikane ndi mchenga wotentha komanso kuti izithamanga kwambiri. Chinthu chinanso chimene chimaithandiza n’chakuti imatha kulondola una wake mosavuta ndiponso mwamsanga isanapserere ndi dzuwa.