Mawu a M'munsi
a Komabe, iye safunikira chophimba kumutu, pamene alalikira kunyumba ndi nyumba, chifukwa chakuti thayo la kulalikira mbiri yabwino liri la Akristu onse. Koma ngati mikhalidwe imafunikiritsa kuti achititse phunziro la Baibulo la panyumba pamene mwamuna wake alipo (mutu wake, ngakhale kuti saali Mkristu), ayenera kugwiritsira ntchito chophimba mutu. Ndiponso, ngati, mkhalidwe wapadera, chiwalo chodzipatulira champingo chiripo pamene akuchititsa phunziro la Baibulo la panyumba lolinganizidwa pasadakhale, ayenera kuphimba mutu wake, koma mbaleyo adzayenera kupereka pemphero.