Mawu a M'munsi
a Patapita zaka pafupifupi 60 Yohane atamwalira, munthu wina wa zaka 86 dzina lake Polycarp, anaphedwa mumzinda wa Simuna powotchedwa chifukwa chokana kusiya kukhulupirira Yesu. Buku linalake lofotokoza za kuphedwa kwa Polycarp, lomwe anthu amakhulupirira kuti linalembedwa m’nthawi imene iye anaphedwa, linanena kuti pamene anthu ankasonkhanitsa nkhuni zomuwotchera, “monga mwa chizolowezi chawo, Ayuda anajijirika kwambiri pothandizira pa ntchitoyi.” Iwo anachita zimenezi ngakhale kuti limeneli linali “tsiku la Sabata lapadera.”—The Martyrdom of Polycarp.