Mawu a M'munsi
b Magazini a Nsanja ya Olonda, amene amafalitsidwa ndi Akhristu odzozedwa, akupitiriza kusonyeza kufunika kogwiritsira ntchito mpata umenewu mwamsanga ndi kugwira nawo mokwanira ntchito yolalikira. Mwachitsanzo, onani nkhani yakuti “Sangalalani ndi Ntchito Yopanga Ophunzira” mu Nsanja ya Olonda ya January 15, 2009, komanso yakuti “Khalani Maso” mu Nsanja ya Olonda ya March 15, 2009, ndi yakuti “Khalani ‘Achangu pa Ntchito Zabwino’” mu Nsanja ya Olonda ya June 15, 2009. Pa avereji, m’chaka cha 2010 panali anthu okwana 1,132,861 amene anachita utumiki wa upainiya.