Mawu a M'munsi
c Buku lina linanena kuti: “Zipolowe zimene ansembe achikunja ankayambitsa, zinachititsa kuti mafumu adziwe zambiri zokhudza Chikhristu. Ansembewo ankayambitsa zipolowezo chifukwa cha mantha poona kuti Chikhristucho chinkafalikira mofulumira. Choncho Trajan [98-117 C.E.] anakakamizika kukhazikitsa malamulo amene cholinga chake chinali kuthetsa pang’onopang’ono kufalikira kwa ziphunzitso zatsopano zimene zinkasintha anthu n’kuwachititsa kuyamba kudana ndi kulambira milungu. Pa nthawi imene Pliny Wamng’ono anali bwanamkubwa wa dera la Bituniya [limene kumpoto kwake linachita malire ndi chigawo cha Asia cholamuliridwa ndi Aroma], ankafunikira kuweruza nkhani zambiri zovuta zokhudzana ndi Chikhristu chimene chinkafalikira mofulumira kwambiri. Komanso ankafunikira kuthetsa mkwiyo umene anthu achikunja am’derali anali nawo chifukwa cha kufalikira kwa Chikhristucho.”—McClintock and Strong’s Cyclopedia (Volume X, page 519).