Mawu a M'munsi
b Mawu akuti ‘phompho’ (Chigiriki, aʹbys·sos; Chiheberi, tehohmʹ) amatanthauza malo ophiphiritsa amene munthu kapena chinthu chomwe chili kumeneko sichingathe kuchita chilichonse. (Onani Chivumbulutso 9:2.) Koma mawuwa angatanthauzenso nyanja yaikulu. Mawu achiheberiwo kawirikawiri amawamasulira kuti “madzi akuya.” (Salimo 71:20; 106:9; Yona 2:5) Choncho “chilombo chotuluka muphompho” n’chimodzimodzi ndi ‘chilombo chotuluka m’nyanja.’—Chivumbulutso 11:7; 13:1.