Mawu a M'munsi
c Tikafufuza zimene zinachitikira anthu a Mulungu pa nthawiyi, zikuoneka kuti masiku atatu ndi hafu amenewa si nthawi yeniyeni ya maola 84, ngakhale kuti miyezi 42 ikuimira zaka zenizeni zitatu ndi hafu. N’kutheka kuti nthawi ya masiku atatu ndi hafu, yomwe inayamba zaka zitatu ndi hafu zitatha, yatchulidwa kawiri (pa vesi 9 ndi 11) posonyeza kuti ndi nthawi yaifupi poyerekezera ndi zaka zenizeni zitatu ndi hafu zimene mbonizo zinkagwira ntchito zili pa mavuto ambiri.