Mawu a M'munsi
d Tingayerekezere zimenezi ndi gulu la kapolo wokhulupirika ndi wanzeru limene limapereka chakudya kwa antchito apakhomo pa nthawi yoyenera. (Mateyu 24:45) Gulu la kapoloyu lili ndi udindo wopereka chakudya, koma antchito apakhomo, omwe ndi munthu aliyense amene ali m’gulu la kapoloyo, amalimbikitsidwa akamadya chakudya chauzimu chimenecho. Choncho magulu awiri onsewa akunena za anthu omweomwewo, kungoti pena awafotokoza ngati gulu, pena ngati munthu mmodzimmodzi.