Mawu a M'munsi
a Kadinala wina wa Katolika amene anakhalapo m’zaka za m’ma 1800, dzina lake John Henry Newman, analemba m’buku lake mfundo zosonyeza kuti miyambo ndi ziphunzitso zambiri za Matchalitchi Achikhristu ampatuko zinachokera ku zipembedzo zachikunja. Iye analemba kuti: “Pali zinthu zambiri zochokera kuchikunja zimene tchalitchi chinangozitenga n’kuyamba kuziona ngati zoyera. Zina mwa zinthu zimenezi ndi monga kugwiritsira ntchito akachisi, kupatulira akachisi amenewa kwa oyera enaake, komanso kumawakongoletsa nthawi zina ndi nthambi za mitengo; kugwiritsira ntchito zofukiza, nyale ndi makandulo; kupereka mapemphero othokoza chifukwa choti munthu wachira; kugwiritsira ntchito madzi oyera; kuchita m’bindikiro; kukhala ndi masiku komanso nyengo zopatulika; kugwiritsira ntchito makalendala, kuyendera limodzi mumsewu monga gulu, kudalitsa minda; kukhala ndi zovala zapadera za ansembe, kumeta ansembe, mphete ya ukwati, kuyang’ana Kum’mawa, kugwiritsira ntchito zifaniziro kumene kunayamba chaposachedwa, mwinanso mawu amene ansembe amanena mobwerezabwereza, komanso nyimbo yakuti ‘Ambuye, Mutichitire Chifundo.’”—Essay on the Development of Christian Doctrine.
M’malo moona kuti kupembedza mafano koteroko n’koyera, “Yehova Wamphamvuyonse” amalimbikitsa Akhristu kuti: “Tulukani pakati pawo, lekanani nawo, . . . musakhudze chinthu chodetsedwa.”—2 Akorinto 6:14-18.