Mawu a M'munsi
a Malemba ena amanena kuti Yesu anali m’Manda pa nthawi imene anali wakufa. (Machitidwe 2:31) Komabe tisaganize kuti nthawi zonse tanthauzo la mawu akuti Manda limafanana ndi tanthauzo la mawu akuti phompho. Baibulo limatiuza kuti Satana komanso chilombo adzaponyedwa kuphompho. Koma limasonyeza kuti amene amapita ku Manda ndi anthu okha ndipo amagona mu imfa, kuyembekezera kudzaukitsidwa.—Yobu 14:13; Chivumbulutso 20:13.