Mawu a M'munsi
a Ponena za ana a m’mabanja a zipembedzo zosiyana, Steven Carr Reuben, Ph.D., m’buku lake lakuti Raising Jewish Children in a Contemporary World, akuti: “Ana amasokonezeka pamene makolo amakhala ndi moyo wobisa zimene iwo ali kwenikweni, wosokoneza, wamseri, ndi wopeŵa nkhani za chipembedzo. Pamene makolo ali omasuka, oona mtima, ofotokoza bwino zikhulupiriro zawo, miyezo, ndi za mapwando awo, ana amakula ndi chisungiko ndi odzimva kukhala ofunika mumkhalidwe wa chipembedzo umene uli wofunika kwambiri pa kukula kwa chidaliro chawo ndi chidziŵitso ponena za malo awo m’dziko.”