Mawu a M'munsi
a M’maiko ena, muli malo ochiritsira, zipatala, ndi maprogramu ochiritsa amene amathandiza zidakwa ndi mabanja awo. Kaya muyenera kufuna chithandizo choterocho kapena ayi ndi nkhani yaumwini. Watch Tower Society simasankhira munthu mtundu uliwonse wa kuchiritsa. Komabe, payenera kukhala kusamala, kuti pofuna chithandizo, munthu asadziloŵetse m’machitidwe amene amaswa mapulinsipulo a Malemba.