Mawu a M'munsi
c Buku lakuti Textual Criticism of the Hebrew Bible, lolembedwa ndi Emanuel Tov, likunena kuti: “Mwa kuupima ndi carbon 14, 1QIsaa [Mpukutu wa Yesaya wa ku Nyanja Yakufa] wapezeka kuti ngwapakati pa 202 ndi 107 BCE (kutsata kalembedwe kake: ngwa mu 125-100 BCE) . . . Njira yotsata kalembedwe kake imene yatchulidwayo, imene aiwongolera pazaka zaposachedwapa, imenenso imalola kupeza deti lenileni mwa kuyerekezera mpangidwe ndiponso kaimidwe ka zilembo zake ndi zinthu zina zonga makobiri ndi zozokota zokhala ndi madeti, yakhala yodalirika ndithu.”6