Mawu a M'munsi
a Pali umboni wodalirika wakuti mabuku a m’Malemba Achihebri—kuphatikizapo la Yesaya—analembedwa kale kwambiri zisanayambe zaka za zana loyamba C.E. Wolemba mbiri Josephus (m’zaka za zana loyamba C.E.) anatero kuti mpambo wa mabuku ovomerezedwa a m’Malemba Achihebri unali utakhazikitsidwa kalekale masiku ake asanafike.8 Ndiponso, Baibulo lachigiriki la Septuagint, matembenuzidwe a Malemba Achihebri m’Chigiriki, linayambidwa m’zaka za zana lachitatu B.C.E. ndipo linamalizidwa podzafika zaka za zana lachiŵiri B.C.E.