Mawu a M'munsi
a Ngakhale kuti mngeloyu sakutchulidwa dzina, zikuoneka kuti ndi mmodzimodziyo amene mawu ake anamveka akulangiza Gabrieli kuti athandize Danieli pom’fotokozera masomphenya amene anaona. (Yerekezani Danieli 8:2, 15, 16 ndi 12:7, 8.) Ndiponso, Danieli 10:13 amasonyeza kuti Mikaeli, “wina wa akalonga omveka,” anafika kudzathandiza mngelo ameneyu. Choncho, mngelo wosatchulidwa dzina ameneyu ayenera kuti ali ndi mwayi wogwira ntchito limodzi ndi Gabrieli komanso ndi Mikaeli.