Mawu a M'munsi
b Ulosi wa pa Danieli chaputala 11 suneneratu mayina a maulamuliro andale amene amatenga malo a mfumu ya kumpoto ndi mfumu ya kumwera pa nthaŵi zosiyanasiyana. Mayinawo amadziŵika kokha pamene zochitikazo ziyamba kuoneka. Ndiponso, popeza kuti mkanganowo umachitika m’zigawozigawo, zimakhalapo nyengo zina zimene kulimbanako kumalekeka—mfumu ina imalamulira pamene inayo imangokhala.