Mawu a M'munsi
b Ena amaganiza kuti kale anthu ankagwiritsa ntchito chipangizo chachikale choonera zinthu zomwe zili kutali. Iwo amati, kodi anthu a nthawi imeneyo paokha akanadziwa bwanji kuti nyenyezi zilipo zambiri ndipo n’zosawerengeka? Koma amanyalanyaza mfundo yoti Yehova, yemwe ndi Mlembi wamkulu wa Baibulo, ndi amene ankathandiza anthuwo kudziwa zimenezi.—2 Timoteyo 3:16.