Mawu a M'munsi
a Mawu akuti “mwana wamasiye” akusonyeza kuti Yehova amadera nkhawa kwambiri ana onse amasiye, kaya aamuna kapena aakazi. Yehova anaonetsetsa kuti m’Chilamulo mwalembedwa zokhudza chigamulo chomwe chinaperekedwa pa nkhani ya ana aakazi a Tselofekadi omwe anali amasiye. Chigamulo chimenechi chinakhala lamulo ndipo chinkateteza ufulu wa ana aakazi amasiye.—Numeri 27:1-8.