Mawu a M'munsi
b Mu akachisi a Akanani munkakhala zipinda zapadera zoti azichitiramo zachiwerewere koma Chilamulo cha Mose chinkanena kuti anthu odetsedwa asamalowe n’komwe m’kachisi. Choncho popeza kugonana kunkachititsa munthu kukhala wodetsedwa kwa kanthawi, palibe amene mwalamulo akanachititsa kuti kugonana kukhale mbali ya kulambira panyumba ya Yehova.