Mawu a M'munsi
a Mobwerezabwereza Baibulo limasonyeza kuti pali kugwirizana pakati pa chiyembekezo choti akufa adzauka ndi zimene Yehova amakumbukira. Munthu wokhulupirikayo Yobu anauza Yehova kuti: “Zikanakhala bwino mukanandiikira nthawi n’kudzandikumbukira.” (Yobu 14:13) Yesu anatchula za kuukitsidwa kwa “onse amene ali m’manda achikumbutso.” Izi zinali zoyenera chifukwa Yehova amawakumbukira bwino kwambiri akufa amene akufuna kudzawaukitsa.—Yohane 5:28, 29.