Mawu a M'munsi
b Palembali, Mabaibulo ena anamasulira kuti munthu amene akukhudza anthu a Mulungu ndiye kuti akudzikhudza yekha diso lake kapena akukhudza diso la Aisiraeli, osati la Mulungu. Kulakwitsa kumeneku anakuyambitsa ndi anthu ena okopera Malemba amene ankaganiza kuti vesili likunyoza Mulungu. Koma maganizo awo olakwikawa anachititsa kuti mfundo yoti Yehova amachitira kwambiri chifundo anthu ake isaonekere.