Mawu a M'munsi
a Mawu achiheberi amene anawamasulira kuti “amakhululukira machimo,” amatanthauza “kulambalala machimo.” Katswiri wina wa Baibulo anafotokoza kuti mawu amenewa “anachokera ku zimene munthu wapaulendo amachita pongolambalala chinthu chomwe alibe nacho chidwi. Choncho Mulungu amaona ndithu machimo athu koma nthawi zina sawalabadira n’komwe. Iye amachita zimenezi popeza amakhululuka.”