Mawu a M'munsi
a Ulosi umenewu uyenera kuti unakwaniritsidwa koyamba pa nthawi ya Amakabeo. Pa nthawiyi Ayuda, motsogoleredwa ndi Amakabeo, anapirikitsa adani awo m’dziko la Yuda ndipo anapanganso mwambo wopereka kachisi kwa Mulungu. Zimenezi zinathandiza Ayuda ena kuti athe kulandira Mesiya pa nthawi imene anaonekera.—Danieli 9:25; Luka 3:15-22.