Mawu a M'munsi
a Mawu a Chigiriki amene anawamasulira kuti “chitsanzo,” kwenikweni amatanthauza “pepala lokhala ndi zilembo limene linkaikidwa pansi pa pepala lina limene ankafuna kulembapo.” Pa anthu onse amene anauziridwa kulemba Malemba a Chigiriki, mtumwi Petulo yekha ndi amene anagwiritsa ntchito mawu amenewa ndipo anthu ena amanena kuti mawuwa amatanthauza “‘pepala lokhala ndi zilembo’ limene mwana amene akuphunzira kulemba ankaika pansi pa pepala lina kuti azilemba motsatira zilembozo ndipo amayesetsa kuti zifanane ndendende.”