Mawu a M'munsi
c Mawu akuti ‘olemetsa’ anagwiritsidwanso ntchito pa Mateyu 23:4, pofotokoza za “akatundu olemera,” omwe ndi miyambo ya anthu komanso malamulo ambirimbiri amene alembi ndi Afarisi ankakakamiza anthu wamba kuti azitsatira. Mawu omwewanso anatanthauziridwa kuti ‘kupondereza’ pa Machitidwe 20:29, 30, ndipo amanena za ampatuko opondereza amene anayamba “kulankhula zinthu zopotoka” pofuna kusocheretsa ena.