Mawu a M'munsi
a Ena mwa anthu otsutsawa anali a m’gulu lotchedwa “Sunagoge wa Omasulidwa.” N’kutheka kuti iwo anagwidwa ndi Aroma ndipo kenako anamasulidwa kapena mwina anali akapolo omasulidwa amene analowa Chiyuda. Ena anali ochokera ku Kilikiya, dera limenenso kunkachokera Saulo wa ku Tariso. Nkhaniyi sifotokoza ngati Saulo anali m’gulu la anthu ochokera ku Kilikiyawo, amene sanathe kulimbana ndi nzeru zimene Sitefano anasonyeza.