Mawu a M'munsi
b Nthawi zambiri atumwi ndi amene anali ndi udindo wopereka mphatso ya mzimu woyera kwa anthu ena. Koma pa nthawiyi, zikuoneka kuti Yesu anapatsa Hananiya mphamvu zopereka mphatso ya mzimu kwa Saulo. Saulo atakhala wokhulupirira, panapita nthawi yaitali ndithu asanakumane ndi atumwi 12 aja. Komabe, n’kutheka kuti pa nthawi yonseyi iye ankalalikira mwakhama. Choncho Yesu anaonetsetsa kuti Saulo ali ndi mphamvu zimene zingamuthandize kugwira ntchito yolalikira imene anam’patsa.