Mawu a M'munsi
b Dokotala wina amenenso amalemba mabuku, analemba kuti zizindikiro za matenda amene Herode ankadwala, zimene Josephus ndi Luka anafotokoza, ziyenera kuti zinayamba chifukwa cha njoka za m’mimba zimene zinadzaza m’matumbo mwake. Nthawi zina munthu amatha kusanza njoka za m’mimbazo, kapena zimatuluka m’thupi lake munthuyo akafa. Buku lina linati: “Zimene Luka anafotokoza mwatsatanetsatane monga dokotala zokhudza imfa ya [Herode], zikusonyeza kuti imfayi inali yochititsa mantha.”