Mawu a M'munsi
f Polankhulapo pa mawu a Paulo akuti ankayenda “dzuwa lili pamutu,” katswiri wina wa Baibulo ananena kuti: “Munthu amene anali pa ulendo ankafunikira kupuma nthawi ya masana chifukwa kunkatentha kwambiri. Koma ngati sanapume, zinkasonyeza kuti akufulumira kwambiri. Choncho apa tikuona kuti Paulo ankadzipereka kwambiri pa ntchito yozunza Akhristu.”