Mawu a M'munsi
a Paulo ankafuna kuti amusungebe Onesimo, koma kuchita zimenezi kukanakhala kuphwanya malamulo a Aroma komanso kukanakhala kumuphwanyira ufulu Filimoni, amene anali Mkhristu komanso mbuye wake wa Onesimo. Choncho Onesimo anabwerera kwa Filimoni, atatenga kalata yochokera kwa Paulo. M’kalatayo, Paulo analimbikitsa Filimoni kuti amulandire bwino Onesimo kapolo wake, amene tsopano analinso m’bale wake wauzimu.—Filim. 13-19.