Mawu a M'munsi
a Baibulo lina lachingelezi limene linasindikizidwa mu 2005 (NET Bible) palemba limeneli limati: “Musafanane ndi dzikoli.” Pofotokoza mmene munthu angafananire ndi dzikoli, mawu a m’munsi a pavesi limeneli, amati: “Pali zinthu ziwiri zimene zimachititsa munthu kuti afanane ndi dzikoli. Choyamba, dziko limachititsa munthuyo kuti afanane nalo iye asakudziwa, ndipo pa nthawi yomweyo, munthuyo amachita kufuna yekha kuti afanane nalo. Choncho zikuoneka kuti nthawi zambiri kuti munthu afike pofananadi ndi dzikoli, zinthu ziwiri zonsezi zimachitika nthawi imodzi.”